Sunday, January 9, 2011

MULUNGU ATATE


2.0. ZOYENERA KUDZIWA:
 Chikhalidwe cha Mulungu
 Kodi Mulungu ndi ndani?
 Ukulu wa Mulungu
 Chilengedwe
 Chimene ife tiri pamaso pa Mulungu
 Kukhulupirira Mulungu

2.1. MULUNGU ATATE.
Mulungu ndi chikondi ndipo ndi Mlengi wa zonse. Iye alibe malire. Ndi chinthu chovuta kwambiri kuti tifotokoze maonekedwe ake a Mulungu. Iye alibe chiyambi ndipo alibe mathero; amafikira dziko lonse lapansi. Ngakhale kuti Iye amakhala Kumwamba, mphamvu zake zimaonekera Kumwamba ndi dziko lonse lapansi. Ife tonse tidalengedwa ndi mphamvu zake (Yobu 11:7, Yesaya 66:1, Masalimo 139, 47:8, Genesisi 1).

2.2. CHIKHALIDWE CHA MULUNGU.

2.2.1. Woyera:
Mulungu ndiye mwini chiyero. Iye amakhala m’chiyero nthawi zonse ndipo chiyero chake chimaonekera kwa ana ake amene amachita chifuniro chake. Onse okhulupirira Mulungu magawana chiyero chake mwa Mzimu Woyera (1 Samuele 2:2, Levitiko 19:2, 2 Mbiri 20:21, Masalimo 29:2, Mateyu 5:48, 19:16-19, Aroma 11:22, 15:16, Aheberi 12:10,14, 1 Petro 1:16, Chivumbulutso 15:4).

2.1.2. Wolungama:
Mulungu sakondwera ndi machimo. Iye sakhala mu uchimo. Anthu onse omutsatira Iye akuyenera kuyenda m’chilungamo chake nthawi zonse ndi kudana nacho chinyengo chiri chonse (Yobu 34:12, Masalimo 7:9, 1 Akorinto 6:9-10, Aheberi 1:8-9, 12:4, 1 Yohane 3:7-9, Chivumbulutso 16:5, 19:2).

2.1.3. Wachikondi ndi chifundo:
Mulungu ndiye chikondi ndipo chikondicho chimayambira kwa Iye. Mwa chikondi chake anatipatsa Mwana wake kutifera pamtanda kuti tipeze chipulumutso. Iye amatichotsera mantha athu onse kuti tionane naye maso ndi maso kudzera m’Mau ake. Chifukwa cha ichi, palibe chotilekanitsa ife ndi Iye ngati tikhala mwa Iye nthawi zonse (Levitiko 19:18, Masalimo 69:16, Maliro 3:22-23, Luka 10:27, Yohane 3:16, Aroma 8:37-39, 1 Akorinto 13:4-7, Agalatiya 5:14, Aheberi 4:16).

2.1.4. Wokhulupirika ndi choonadi:
Mulungu ndi wokhulupirika nthawi zonse. Mulungu amakwaniritsa zonse zimene walonjeza popanda chokaikitsa. Iye sali ngati munthu amene kukhulupirika kwake nkokaikitsa nthawi zonse. Mulungu amakonda munthu wokhulupirika m'zochita zake ndipo amapereka madalitso ake kwa munthu wotere (Yesaya 25:1, Chivumbulutso 3:14, 19:11, Aroma 3:4, Yohane 17:3, Aheberi 10:23, 11:11, 1 Atesolonika 5:23-24, 2 Timoteo 1:12, 1 Akorinto 10:13, Masalimo 31:23, 101:6, Mateyu 25:21).

2.3. Wopereka:
Mulungu mwa chikondi chake amatipatsa ife zinthu zosiyanasiyana kuti zitithandize pamoyo wathu monga:
 Malemba onse a m’Baibulo
 Mwana wake Yesu Kristu
 Mzimu wake Woyera
 Chikhululukiro cha machimo
 Chisomo chake kwa odzichepetsa pamaso pake
 Mpumulo kwa onse olema ndi othodwa
 Nzeru zakuya za uzimu kwa ana ake
 Kupambana koposa padziko lapansi kudzera mwa Kristu
 Kuthekera koposa mu utumiki wake
 Chakudya pamoyo wathu
 Mphamvu zolamulira m’chilungamo chake. Tikhale nao mtima wothandiza anzathu mosanyinyirika ndi mopanda tsankho (Masalimo 136:25, Daniele 2:37, 2:23, Yohane 3:16, Aroma 5:5, 6:23, 8:32, 2 Timoteo 2:25, 1 Petro 4:11, 5:5, Yakobo 1:5, 4:6, 1 Akorinto 15:57, Mateyu 11:28, Luka 11:13, 1 Atesolonika 4:8, Aefeso 3:7, Deuteronomo 8:18).

2.4. UKULU WA MULUNGU.

2.4.1. Amadziwa zonse:
Nzeru za Mulungu nzodabwitsa ndipo nzovuta kuzidziwa ndi kuzimvetsa. Iye amadziwa china chiri chonse pamoyo wathu (Aroma 6:27, Yobu 9:4, 1 Samuele 2:3, Masalimo 139:4-6, Aroma 11:33, Yakobo 3:14-17, 1:5-7, Akolose 1:9, 2:2-3, 3:16, Aefeso 1:17, 1 Akorinto 3:18-20). Nzeru ndi zochita za Mulungu ndi:
 Zopanda chinyengo
 Zimabweretsa mtendere ndi chimvano
 Ziribe ukali ndi ululu
 Zachifundo ndipo zimatiululira chikondi chake osati chilamulo ai
 Ziribe kukondera kwina kuli konse
 Ziribe umadyera mphotho.

2.4.2. Amapezeka pena pali ponse:
Mulungu amapezeka pali ponse ndipo ndi chifukwa chake tikamapemphera timakhala ndi chikhulupiriro kuti zonse zimene tikupempha, zimveka kwa Iye. Palibe amene angathe kubisala kapena kuzemba pamaso pa Mulungu. Ngakhale Iye amapezeka pali ponse, sizikutanthauza kuti amapezekanso mu zinthu zonse ai. Mu zinthu monga izi, Iye sapezekamo:

 Mafano kapena kupembedza Mdierekezi (Yesaya 2:8-11, 20-21, Chivumbulutso 9:20)
 Kupembedza chilengedwe kapena zolengedwa zina (Aroma 1:25).
 Kupembedza Angelo (Akolose 2:18, Chivumbulutso 22:8-9).
 Kupembedza mizimu ya anthu akufa (Levitiko 20:6, Deuteronomo 18:9-11, Yesaya 8:19).

2.4.3. Wamphamvu zonse:
 Iye ndiye Mlengi wa kumwamba ndi dziko (Genesisi 1).
 Mwa Iye, zinthu zonse zidalengedwa ndipo zidakhazikika (Akolose 1:17).
 Mphamvu zake nzochuluka (Yobu 9:4).
 Zinthu zonse ndi zotheka ndi Mulungu (Mateyu 19:26, Yeremia 32:17, 27, 1 Akorinto 1:25, Yoele 3:10, 2 Akorinto 12:10, Aheberi 11:34).

2.4.4. Wamuyaya:
Mulungu alibe malire ndipo adzakhala mpaka muyaya. Iye ndi Woyamba ndi Wotsiriza. Iye adali, ali ndipo adzakhala mpaka nthawi zosatha (Yesaya 43:10, Yohane 3:15-16, Aroma 6:23, 1 Yohane 5:11-13, 20, 2 Timoteo 1:12, Masalimo 90:1-2, Chivumbulutso 22:1-8).

2.4.5. Samasintha:
Mulungu ali yemweyo nthawi zonse kotero chikondi chake nchosathanso. Nkoyenera kumkhulupirira ndi kumudalira nthawi zonse (1 Akorinto 15:51-53, Aheberi 13:8, Yakobo 1:17, 1 Yohane 3:2).

2.5. CHILENGEDWE.

2.5.1. Tsiku Loyamba:
Patsiku loyamba Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi. Dziko lapansi lidali lopanda maonekedwe eni eni ndiponso losakonzeka. M’dima udali utaphimba nyanja yaikulu ponse ponse ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo. Mulungu adalamula kuti kuyere ndipo kudatero ndipo kuyerako ndiko masana ndi m’dima ndiwo usiku. Kudali madzulo ndiponso m’mawa pa tsiku loyamba.

2.5.2. Tsiku Lachiwiri:
Mulungu adalekanitsa madzi kuti akhale pa malo awiri olekana. Adalenga cholekanitsa madzi ndipo dzina lake ndilo thambo.

2.5.3. Tsiku Lachitatu:
Mulungu adaika madzi pamalo amodzi kuti mtunda uoneke. Mtundawo ndilo dziko lapansi. Madzi osonkhanitsidwa pamodzi aja ndiwo nyanja. Panthaka padamera zomera zobala njere ndi mitengo yobala zipatso zanjere monga mwa mtundu wake. Padziko padamera zipatso za mitundu yonse.

2.5.4. Tsiku Lachinai:
Mulungu adalenga kuthambo kuti kukhale miyuni iwiri ikulu ikulu kulekanitsa usana ndi usiku. Iyo, idali zizindikiro za nyengo, masiku ndi zaka. Muuni waukulu wowala masana adautcha dzina lake dzuwa ndipo wowala usiku Mwezi. Iye adalenganso nyenyezi za kuthambo.

2.5.5. Tsiku Lachisanu:
M’nyanja mudali zamoyo zambirimbiri komanso mbalame zouluka mlengalenga. M’nyanja mudali nsomba zazikulu pamodzi ndi zolengedwa zina zokhala m’madzi ndiponso mbalame ndi zouluka zina za mitundu mitundu.

2.5.6. Tsiku Lachisanu ndi chimodzi:
Padali mitundu yonse ya zamoyo monga zoweta, zokwawa, ndi nyama zakuthengo potsata mitundu yake. Mulungu adalenga munthu m’chifanizo chake kuti alamulire zolengedwa zonse.

2.5.7. Tsiku Lachisanu ndi chiwiri:
Mulungu adamaliza kulenga zinthu zonse ndipo adapuma. Iye adalidalitsa tsiku limeneli, naliyeretsa chifukwa patsikuli adapuma atatsiriza kulenga zinthu zonse.

2.6. CHIMENE IFE TIRI PAMASO PA MULUNGU.
 Ndife olengedwa ake a Mulungu (Masalimo 139:14-16).
 Ndife ake eni eni a Mulungu (1 Akorinto 6:19-20).
 Ndife oitanidwa kuti timpembedze Mulungu (Chivumbulutso 4:11).

2.7. CHISANKHO CHATHU.
Yesu Kristu adati: “Kondani Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi nzeru zanu zonse ndi mphamvu zanu zonse“(Mateyu 22:37). Munthu adalengedwa kuti atumikire ndi kukonda Mulungu nthawi zonse. Baibulo limatiuza za Yoswa amene adali mtsogoleri wa Aisraeli. Iyeyu adali munthu wamphamvu pa utumiki wake ndipo adatsogolera Aisraeli ndi kupambana nkhondo zimene ankamenyana ndi adani awo. Yoswa adauza Aisraeli kuti adzisankhire okha womtumikira koma iye ndi banja lake adasankha kutumikira Mulungu ngakhale zinthu zitavuta bwanji (Yoswa 24:15). Lero lino chisankho chimenechi chikubwera kwa ife. Kodi timdzamtumikira Mulungu kapena zochita zathu zikutilekanitsa ife kuyandikana naye Atate wathu.


Download Pdf version from here!

God Bless you!

BAIBULO


1.1.1. ZOYENERA KUDZIWA:
 Baibulo ndi chiani
 Cholinga cha Baibulo
 Zimene Baibulo limafotokoza
 Amene adalemba Baibulo
 Mwini wake Baibulo
 Kufunika kwa Baibulo
 Oyenera kuwerenga ndi kugwiritsa ntchito Baibulo
 Chiyembekezo cha Mkristu

1.1.2. KODI BAIBULO NDI CHIANI?
Baibulo ndi Mau a Mulungu ndipo ndi Bukhu Lopatulika kwambiri pa mabuku onse. Bukhuli lidalembedwa ndi anthu osiyanasiyana amene adatsogozedwa ndi Mzimu Woyera (2 Timoteo 3:16). Ngakhale Baibulo liri mabukhu okwana 66 mkati mwake, mutu wake ndi umodzi basi: “Chikonzero cha Mulungu chopulumutsa dziko lapansi”. Bukhuli liri ndi zigawo ziwiri: “Chipangano Chakale ndi Chiangano Chatsopano”. Chipangano Chakale chiri ndi mabuku 39 ndipo Chipangano Chatsopano chiri ndi 27 potsatira Bukhu limene lalembedwa kuti: “Bukhu Lopatulika- Mulungu Anena Masiku Ano”.

1.1.3. LONJEZO LOPAMBANA.
Lonjezo lopambana limene Baibulo limatiululira ndi Moyo Wosatha kudzera mwa Mwana wake Yesu Kristu. Mulungu adalonjeza Moyo Wosatha ngati tikhulupirira Yesu Kristu kukhala Mbuye ndi Mpulumutsi wa moyo wathu nthawi zonse (Yohane 3:16).

1.1.4. CHOLINGA CHA BAIBULO.
Cholinga cha Mau a Mulungu kwa ife ndi kufuna kutiunikira njira yopita kumwamba kwa Atate. Mau a Mulungu ali pakati pathu kutidzudzula, kutikonza, kutiphunzitsa ndi kutipatsa nzeru zochuluka zakuya mu uzimu kuti chikhulupiriro chathu mwa Kristu chikule koposa (2 Timoteo 3:15-16, 2 Petro 1:3-4).

1.1.5. KUWERENGA BAIBULO.

Tiyenera kuwerenga Baibulo pa zifukwa izi:

1.1.5.1. Kuti tikule mu Uzimu:
Mau a Mulungu ndi chakudya chimene chimapereka thanzi ku moyo wathu kuti tikule ndi nzeru zoopa Mulungu nthawi zonse ndipo moyo wathu umakhala wokhathamira ndi madalitso ake pamene tisunga ndi kugwiritsa ntchito Mau ake m’moyo wathu (Yeremia 15:16, Ezekiele 3:1-3, 1 Petro 2:2, 1 Akorinto 3:1-2, Aheberi 5:12-14).

1.1.5.2. Kuti tipewe machimo:
Mau a Mulungu amatitsogolera ife ku njira yoongoka pamaso pa Mulungu ndipo amabweretsa chiyero pakati pathu kuti tipewe machimo ndi machenjerero a Satana woipayo (Masalimo 119:9-11,133, Yesaya 59:1).

1.1.5.3. Kuti tikhale ndi moyo wabwino ndi thanzi:
Kumvera Mau a Mulungu kumachititsa kuti munthu akhale ndi moyo wabwino komanso kuchira kumatenda aku thupi ndi uzimu (Eksodo 15:26, Masalimo 107:20, 119:50).

1.1.5.4. Kuti tikhale ndi chuma choposa:
Mulungu adalonjeza kukhala ndi moyo wosasowa kanthu m’moyo wathu wa uzimu ngati timutsatira Iye m’choonadi. Tiyenera kuwerenga Mau ake kuti tidziwe ndi kupeza chuma cha mtengo wa patari chimene Mulungu watisungira pochita chifuniro chake (Yoswa 1:8, Masalimo 1:1-3).

1.1.5.5. Kuti tithandizike popemphera:
Mau a Mulungu ndi chida chathu chimene timagwiritsa ntchito popemphera pamaso pake kuti tisasowe chomuuza (Yohane 15:7).

1.1.5.6. Kuti tipeze mphamvu:
Mau a Mulungu amamanga makoma olimba m’mitima yathu kuti ngakhale zopsinja ndi zotibwezeretsa m’mbuyo zambiri tikumane nazo, tipitebe mtsogolo ndi Chikhulupiriro chathu mwa Mulungu Atate kudzera mwa Mwana wake Yesu Kristu (Mateyu 7:24).

1.1.5.7. Kuti tipeze moyo:
Mau a Mulungu amapereka moyo kwa iwo amene ali akufa mu uzimu kuti atsitsimuke ndi kufika mu ufumu wa Mulungu (Yohane 6:63, Masalimo 33:6,9, Aheberi 11:3).

1.1.7. KODI MU BAIBULO MULI ZOLAKWITSA ZINA ZIRIZONSE?
Baibulo ndi Bukhu Lopatulika pa mabuku onse amene tingawapeze pa dziko lonse la pansi. Mzimu Woyera wa Mulungu anatsogolera atumiki ake osiyanasiyana kuti alembe Bikhuli popanda cholakwitsa china chiri chonse. Mulungu kudzera mwa Mzimu Woyera anatsogolera atumiki amenewa kuti:
 Alembe zokhazo zimene Mulungu anawaunikira kuti alembe
 Alembe Mau onse m’Bukhuli popanda zolakwitsa.

Mulungu mwini wake ndiye amene amateteza mau ake kuti asaonongeke m’njira ina iriyonse. Ichi ndi chifukwa chake anthu onse oomboledwa ndi mwazi wa Kristu amakhulupirira kuti Baibulo ndi Mau eni eni ochokera kwa Mulungu (Yesaya 27:3, 40:8, Mateyu 5:18, 24:35, Yohane 10:35).

1.1.8. MAU A MULUNGU (BAIBULO) AMAFANIZIDWA NDI:

1.1.8.1. Madzi:
Mau a Mulungu amatiyeretsa ndi kutisunga kuti tikhale oyera nthawi zonse. Tikachita chisankho m’moyo wathu kutumikira ndi kuchita chifuniro cha Mulungu, Iye amatiyeretsa ndi kutiteteza ku machismo (Yohane 15:3, Aefeso 5:22-27, Masalimo 119:9-11).

1.1.8.2. Kuwala:
Mau a Mulungu ndi nyale ndipo amatiunikira njira yathu kuti tisayende mumdima wa imfa kotero kuti amatipatsa chidziwitso kuti tisalowe mu uchimo (2 Petro 1:9, Masalimo 119:105, 130).

1.1.8.3. Chakudya:
Mau a Mulungu ndi chakudya cha moyo wathu wa uzimu kuti tikule ndi thanzi lolemekeza ndi kutumikira Mulungu nthawi zones (1 Akorinto 3:1-2, 1 Petro 2:2. Aefeso 4:12-15, Yohane 6:20).

1.1.8.4. Mbeu:
Mau a Mulungu ndi mbeu imene ikalowa ndi kukhazikika mkati mwa mtima wathu, imakula ndi kubereka zipatso za uzimu pamaso pa Mulungu. Pa chifukwa ichi, moyo wathu umakhala wopindulitsa koposa pamaso pa Mulungu (Luka 8:14-15, Masalimo 1:3, 2 Akorinto 9:10, 1 Petro 1:23).

1.1.8.5. Lupanga:
Mau a Mulungu ndi Lupanga komanso chida cholimba chothamangitsira nacho Satana. Mwachitsanzo, Kristu adagwiritsa ntchito Mau a Mulungu pogonjetsa Satana m’chipululu muja (Luka 4:1-14, Aefeso 6:17, Aheberi 4:12).

1.1.8.6. Moto:
Mau a Mulungu amaotcha maganizo ndi malingaliro oipa ndipo amatiunikira kuti tikule ndi malingaliro amene achitira ubwino dzina la Mulungu wathu (Yeremia 23:29).

1.1.8.7. Mkaka:
Mau a Mulungu amapereka thanzi kuti tikule ndi moyo wokhathamira ndi madalitso a Mulungu ndiponso moyo wopanda nkhawa ndi mavuto a dziko lapansi (1 Petro 2:2).

1.1.8.8. Uchi:
Mau Mulungu amakoma ngati uchi tikamawerenga chifukwa nthawi ndi nthawi amativumbulutsira zinsinsi zatsopano pa moyo wathu wa uzimu (Masalimo 19:10).

1.1.8.9. Golide:
Mau a Mulungu ndi chuma choposa zina zonse chimene chimapezeka ngati munthu akhulupirira Yesu Kristu ngati Mbuye ndi Mpulumutsi wa moyo wake (Yeremia 19:10).

1.1.8.10. Kalilole (Galasi):
Mau a Mulungu limationetsa chithunzithunzi cha ufumu wa Kumwamba tikatsegula maso ndi mitima yathu kuti Mau’wo akhale mkati mwathu. Amationetseranso malonjezo oposa amene Mulungu watiikira pa moyo wathu (Yakobo 1:23-25).

1.1.8.11. Nyundo (Hamala):
Mau ake Mulungu amaswa makoma onse a uchimo amene ali mkati mwathu ndipo amatithandizanso kuti tiswe malingaliro oipa mkati mwathu (Yeremia 23:29).

1.1.9. MAGAWO AMENE BAIBULO LAFUNGATIRA:

1.1.9.1. Chilamulo:
Mabuku a chilamulo ndi mabuku asanu oyambirira m’Chipangano Chakale kuyamba ndi Genesisi mpaka Deuteronomo. Mulungu adapereka Malamulo osiyanasiyana okhudza moyo wathu wa tsiku ndi tsiku. Choncho, kuwerenga ndi kumvetsa Malamulo ake kungapindulutse miyoyo yathu pamaso pa Mulungu.

1.1.9.2. Mbiri:
Mbiri ndi nkhani kapena zochitika zikulu zikulu zochititsa chidwi zimene zimachitika pa moyo wathu watsiku ndi tsiku. Baibulo limafotokoza zinthu zosiyanasiyana zimene zidachitika kuti ife titengepo phunziro. Mabuku ofotokoza mbiri m’Chipangano Chakale ndi Yoswa mpaka Estere ndipo m’Chipangano Chatsopano ndi Mateyu mpaka Machitidwe a Atumwi.

1.1.9.3. Luntha:
Luntha ndi chimangiriro cha luso ndi nzeru zoposa zimene Mulungu adationetsera kudzera mwa atumiki ake osiyanasiyana kuti tiphunzire ndi kutakasidwa m’mitima yathu pamaso pake. Mabuku amene amafotokoza za luntha ndi Yobu mpaka Nyimbo ya Solomo m’Chipangano Chakale.

1.1.9.4. Ulosi:
Mabuku a Ulosi ndi Yesaya mpaka Malaki m’Chipangano Chakale. Mchipangano Chatsopano bukhu la Chivumbulutso komanso magawo ena a mabuku a Mateyu, Mariko, Luka ndi Yohane ali ndi mau a ulosi. Mabuku amenewa amatiphunzitsa ndi kutiululira chikonzero cha Mulungu pamoyo wathu watsopano ndi mtsogolo (Chivumbulutso 20:4, 1 Akorinto 6:2).

1.1.9.5. Chikhalidwe:
Baibulo limationetsa chikhalidwe chabwino chimene tingatsatire pamoyo wathu. Izi zikuonetsedwa kwambiri m’Chipangano Chatsopano komanso m’mabuku ena m’Chipangano Chakale monga Miyambo ndi Mlaliki.

1.2.0. KUDZIWA ZIMENE BAIBULO LIKUPHUNZITSA.
Poyamba peni peni tikuyenera kudziwa kuti Mau onse opezeka m’Baibulo adalembedwa kuti ife tikhulupirire kuti Yesu Kristu ndiye Wolonjezedwa uja ndipo zonse zidalembedwa kumuchitira Iye umboni (Yohane 20:31, Luka 24:44). Tingadziwe zimene Baibulo likuphunzitsa kudzera m’njira monga izi:

1.2.0.1. Kudzera m’mavumbulutso a Mzimu Woyera:
 Pezani nthawi yabwino yoti muthe kukhala pansi ndikulingalira Mau a Mulungu.
 Funsani Mzimu Woyera kuti akuphunzitseni ndi kudzodza koyenera (Yohane 14:26, 1 Akorinto 2:12-14, 
    Yohane 2:27).
 Pempherani kuti zotchinga za Woipayo zichoke m’moyo wanu kuti mukhale ndi chidziwitso pa Mau ake (2 
    Akorinto 3:14-16).
 Pempherani kuti Mzimu Woyera akupatseni ndi kutsegula chidziwitso chanu (Luka 24:25-27,44-45).
 Pempherani kuti Mzimu wachidziwitso ndi nzeru zoposa komanso mavumbulutso akhale pa inu pamene 
    mukuwerenga Baibulo lanu (Aefeso 1:17-19).

1.2.0.2. Kuwerenga Mau a Mulungu nthawi ndi nthawi:
 Pezani nthawi yosachepera mphindi 30 tsiku ndi tsiku kuti muwerenge Baibulo.
 Werengani Salimo imodzi patsiku ndipo mudzakhala mutawerenga Masalimo onse kawiri pachaka.
 Werengani mutu umodzi m’bukhu la Miyambo patsiku ndipo mudzakhala mutawerenga bukhu lonse la 
    Miyambo kamodzi pamwezi.
 Werengani masamba atatu m’Chipangano Chakale patsiku ndipo mudzakhala mutawerenga Chipangano 
    chonse Chakale kamodzi pachaka.
 Werengani masamba atatu patsiku m’Chipangano Chatsopano ndipo mudzakhala mutawernga Chipangano 
     chonse katatu pachaka.
 Nthawi imene mungasankhe kuwerenga Baibulo lanu ilibe kanthu kweni kweni koma m’mamawa ndi 
    madzulo ndiye nthawi zimene bongo wa munthu umakhala wokonzeka Kulandira zinthu (Masalimo 3:5, 
   4:8).
 Werengani Baibulo lanu mofatsa ndi mosamalitsa. Musathamange. Lingalirani zonse zimene mukuwerenga 
     bwino lomwe.
 Pempherani kwa Mulungu kuti akuunikireni zonse zimene mukufuna kuti mudziwe kuchoka m’Baibulo. 
    Palibe wina amene angamasulire Baibulo momveka bwino kuposa Mulungu mwini wake.
 Powerenga lolani kuti Mulungu akulankhuleni mkati mwa mtima wanu. Dziwani kuti Baibulo lidalembedwa 
    kwa inu. Ngati pali uthenga, uthengawo ukupita kwa inu. Ngati pali chenjezo, chenjezolo likupita kwa inu 
    osati munthu wina ai. Chimodzomodzinso lonjezo kuti zikuchitireni inu ubwino wonse (Agalatiya 2:20).
 Mukatsiriza kuwerenga, pempherani kuti Mulungu amangirire zonse mkati mwa mtima wanu. Sungani 
    pamtima magawo amene akukhudzani kwambiri ndipo muwalingalire mozama. Mulungu adzakudalitsani 
    koposa (Masalimo 119:11).




God bless you!

People Who Believe In The Power Of Prayer

In one of the messages in my Facebook inbox, I found this message lying there for me. I went through it and found it worth sharing with all of you who will one day stumble upon this webpage. I am indebted to sender sender of this message, Pastor Joe Wood and all this message is his work. I am reprinting this with due regard that God's Word is worth sharing. I hope you will enjoy it!

We want to help you develop a deeper and more meaningful relationship with God, the creator of the universe, and have prepared a month of free resources to help you.

When you commit to seeking His face you will receive 5 relevant and applicable messages, 30 days of daily devotionals, and one praise and worship song from the Noise band. 

2 Chronicles 7:14 says, “Then if my people who are called by my name will humble themselves and pray and seek my face and turn from their wicked ways, I will hear from heaven and will forgive their sins and restore their land.” 

The "Seek Your Face" journey is a call to action. It is an invitation for people from all walks of life to go on a journey of discovery. It begins as an adventure that quickly becomes a life long quest until we see Him face to face. As you begin it won't take you long to realize that the goal, the prize, the quest is not a thing, but a Person. 

So what are you waiting for? Sign up and begin the interactive journey of seeking God with people from all around the world today. Register at http://Zyxter.com/

Pastor Joe Wood

P.S. Are you or someone you know in need of prayer? Are you a prayer warrior? If so, join us LIVE right now at http://ZyxterPrayer.com/ for our LIVE prayer broadcast where people from all over the world are assembled to pray and be prayed for!